Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 14:7-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pita pamaso pa munthu wopusa,Sudzazindikira milomo yakudziwa.

8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11. Nyumba ya oipa idzapasuka;Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13. Ngakhale m'kuseka mtima uwawa;Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14. Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace;Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15. Wacibwana akhulupirira mau onse;Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16. Wanzeru amaopa nasiya zoipa;Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17. Wokangaza kukwiya adzacita utsiru;Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18. Acibwana amalandira colowa ca utsiru;Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19. Oipa amagwadira abwino,Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

20. Waumphawi adedwa ndi anzace omwe;Koma akukonda wolemera acuruka.

21. Wonyoza anzace acimwa;Koma wocitira osauka cifundo adala.

22. Kodi oganizira zoipa sasocera?Koma akuganizira zabwino adzalandira cifundo ndi ntheradi.

23. M'nchito zonse muli phindu;Koma kulankhula-lankhula kungopatsa umphawi.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 14