4. Popanda zoweta modyera muti see;Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.
5. Mboni yokhulupirika sidzanama;Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.
6. Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.
7. Pita pamaso pa munthu wopusa,Sudzazindikira milomo yakudziwa.
8. Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace;Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.
9. Zitsiru zinyoza kuparamula;Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.
10. Mtima udziwa kuwawa kwace kwace;Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.