Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 14:25-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Mboni yoona imalanditsa miyoyo;Koma wolankhula zonama angonyenga.

26. Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;Ndipo ana ace adzakhala ndi pothawirapo.

27. Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,Kupatutsa ku misampha ya imfa.

28. Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;Koma popanda anthu kalonga aonongeka.

29. Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;Koma wansontho akuza utsiru.

30. Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;Koma nsanje ibvunditsa mafupa.

31. Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wace;Koma wocitira wosauka cifundo amlemekeza.

32. Wocimwa adzakankhidwa m'kuipa kwace;Koma wolungama akhulupirirabe pomwalira,

33. Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira,Nidziwika pakati pa opusa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 14