1. Mkazi yense wanzeru amanga banja lace;Koma wopusa alipasula ndi manja ace.
2. Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;Koma wokhota m'njira yace amnyoza,
3. M'kamwa mwa citsiru muli ntyole ya kudzikuza;Koma milomo ya anzeru Idzawasunga.
4. Popanda zoweta modyera muti see;Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.
5. Mboni yokhulupirika sidzanama;Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.
6. Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.