Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.

9. Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.

10. Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.

12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.

13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.

15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.

17. Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18. Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.

19. Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,

20. Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 13