Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13:3-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4. Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;Koma moyo wa akhama udzalemera.

5. Wolungama ada mau onama;Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,

6. Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira;Koma udio ugwetsa wocimwa.

7. Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.

8. Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.

9. Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.

10. Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11. Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.

12. Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.

13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 13