Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13:13-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14. Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.

15. Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16. Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.

17. Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa;Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18. Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.

19. Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa;Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,

20. Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21. Zoipa zilondola ocimwa;Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22. Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino;Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.

23. M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 13