Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;Koma wonyoza samvera cidzudzulo.

2. Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.

3. Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4. Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;Koma moyo wa akhama udzalemera.

5. Wolungama ada mau onama;Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,

6. Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira;Koma udio ugwetsa wocimwa.

7. Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.

8. Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 13