Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 13:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;Koma wonyoza samvera cidzudzulo.

2. Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.

3. Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace;Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4. Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu;Koma moyo wa akhama udzalemera.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 13