Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 12:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5. Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.

6. Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 12