10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.
11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.
12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.
13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.
14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.
15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.
16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.
17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.