Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 12:1-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wokonda mwambo akonda kudziwa;Koma wakuda cidzudzulo apulukira.

2. Yehova akomera mtima munthu wabwino;Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,

3. Munthu sadzakhazikika ndi udio,Muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4. Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace;Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5. Maganizo a olungama ndi ciweruzo;Koma uphungu wa oipa unyenga.

6. Mau a oipa abisalira mwazi;Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7. Oipa amagwa kuli zi;Koma banja la olungama limaimabe.

8. Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace;Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9. Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo,Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10. Wolungama asamalira moyo wa coweta cace;Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11. Zakudyazikwanira wolima minda yace;Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12. Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13. M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14. Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15. Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.

16. Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.

17. Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 12