4. Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo;Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.
5. Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.
6. Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.
7. Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka;Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.
8. Wolungama apulumuka kubvuto;Woipa nalowa m'malo mwace.