Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11:23-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24. Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

25. Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26. Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.

27. Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28. Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29. Wobvuta banja lace adzalowa m'zomsautsa;Wopusa adzatumikira wanzeru.

30. Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo;Ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31. Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;Koposa kotani woipa ndi wocimwa?

Werengani mutu wathunthu Miyambi 11