Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pakudza kudzikuza padzanso manyazi;Koma nzeru iri ndi odzicepetsa,

3. Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera;Koma kukhota kwa aciwembu kudzawaononga.

4. Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo;Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

5. Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.

6. Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 11