Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11:19-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Wolimbikira cilungamo alandira moyo;Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20. Okhota mtima anyansa Yehova;Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

21. Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango;Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22. Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23. Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24. Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

25. Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26. Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.

27. Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28. Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 11