Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Woipa alandira malipiro onyenga;Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,

19. Wolimbikira cilungamo alandira moyo;Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20. Okhota mtima anyansa Yehova;Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

21. Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango;Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22. Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23. Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24. Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 11