Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 11:10-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Olungama akapeza bwino, mudzi usekera;Nupfuula pakuonongeka oipa.

11. Madalitso a olungama akuza mudzi;Koma m'kamwa mwa oipa muupasula.

12. Wopeputsa mnzace asowa nzeru;Koma wozindikira amatonthola.

13. Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;Koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14. Popanda upo wanzeru anthu amagwa;Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.

15. Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo;Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.

16. Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;Aukali nagwiritsa cuma.

17. Wacifundo acitira moyo wace zokoma;Koma wankhanza abvuta nyama yace.

18. Woipa alandira malipiro onyenga;Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,

19. Wolimbikira cilungamo alandira moyo;Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20. Okhota mtima anyansa Yehova;Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

Werengani mutu wathunthu Miyambi 11