Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako

9. Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.

10. Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.

11. Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,Tilalire osacimwa opanda cifukwa;

12. Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1