Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:6-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace,Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

7. Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8. Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako

9. Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.

10. Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.

11. Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,Tilalire osacimwa opanda cifukwa;

12. Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.

17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,

20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;

21. Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;

22. Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?Onyoza ndi kukonda kunyoza,Opusa ndi kuda nzeru?

23. Tembenukani pamene ndikudzudzulani;Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,Ndikudziwitsani mau anga.

24. Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1