Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:25-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27. Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28. Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;

29. Cifukwa anada nzeru,Sanafuna kuopa Yehova;

30. Anakana uphungu wanga,Nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31. Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,Nadzakhuta zolingalira zao.

32. Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa acibwana kudzawapha;Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33. Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,Nadzakhala phe osaopa zoipa,

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1