Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:22-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?Onyoza ndi kukonda kunyoza,Opusa ndi kuda nzeru?

23. Tembenukani pamene ndikudzudzulani;Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,Ndikudziwitsani mau anga.

24. Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27. Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28. Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1