16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.
17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;
18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.
19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,
20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;