Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.

17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,

20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1