13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;
15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.
17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;
18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.
19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,
20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;
21. Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;
22. Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu?Onyoza ndi kukonda kunyoza,Opusa ndi kuda nzeru?
23. Tembenukani pamene ndikudzudzulani;Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga,Ndikudziwitsani mau anga.
24. Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;
25. Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.
26. Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;
27. Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.
28. Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;
29. Cifukwa anada nzeru,Sanafuna kuopa Yehova;
30. Anakana uphungu wanga,Nanyoza kudzudzula kwanga konse;
31. Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,Nadzakhuta zolingalira zao.
32. Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa acibwana kudzawapha;Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.