13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;
14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;
15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;
16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.
17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;
18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.
19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,
20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;