Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:12-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13. Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14. Udzacita nafe maere,Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15. Mwananga, usayende nao m'njira;Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16. Pakuti mapazi ao athamangira zoipa,Afulumira kukhetsa mwazi.

17. Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18. Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19. Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere;Cilanda moyo wa eni ace,

20. Nzeru ipfuula panja;Imveketsa mau ace pabwalo;

21. Iitana posonkhana anthu polowera pacipata;M'mudzi inena mau ace;

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1