1. MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.
2. Kudziwa nzeru ndi mwambo;Kuzindikira mau ozindikiritsa;
3. Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe,Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;
4. Kucenjeza acibwana,Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;
5. Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;
6. Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace,Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.
7. Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.
8. Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako
9. Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.