Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Miyambi 1:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.

2. Kudziwa nzeru ndi mwambo;Kuzindikira mau ozindikiritsa;

3. Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe,Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;

4. Kucenjeza acibwana,Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5. Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6. Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace,Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

7. Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8. Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako

Werengani mutu wathunthu Miyambi 1