1. MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.
2. Kudziwa nzeru ndi mwambo;Kuzindikira mau ozindikiritsa;
3. Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe,Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;
4. Kucenjeza acibwana,Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;
5. Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira;Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;