Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 4:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti mitundu yonse ya anthu idzayenda, wonse m'dzina la mlungu wace, ndipo ife tidzayenda m'dzina la Yehova Mulungu wathu ku nthawi yomka muyaya.

6. Tsiku ilo, ati Yehova, ndidzamemeza wakutsimphinayo, ndi kusonkhanitsa wopitikitsidwayo, ndi iye amene ndinamsautsa;

7. ndipo wotsimphinayo ndidzamuyesa wotsala, ndi iye wotayidwa kutali mtundu wamphamvu; ndipo Yehova adzakhala mfumu yao m'phiri la Ziyoni kuyambira pamenepo kufikira kosatha.

8. Ndipo iwe, nsanja ya nkhosa, citunda ca mwana wamkazi wa Ziyoni, udzafikira iwe, inde udzafika ulamuliro wakale, ufumu wa mwana wamkazi wa Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Mika 4