Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Mika 3:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Amanga Ziyoni ndi mwazi, ndi Yerusalemu ndi cisalungamo.

11. Akuru ace aweruza cifukwa ca mphotho, ndi ansembe ace aphunzitsa cifukwa ca malipo, ndi aneneri ace alosa cifukwa ca ndarama; koma atsamira pa Yehova, nati, Kodi Yehova sali pakati pa ife? palibe coipa codzatigwera.

12. Momwemo Ziyoni adzalimidwa ngati: munda cifukwa ca inu, ndi m'Yerusalemu mudzasanduka miunda, ndi phiri la nyumba ngati misanje ya m'nkhalango.

Werengani mutu wathunthu Mika 3