Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 98:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;Kuwitsani ndi kupfuulira mokondwera; inde, yimbirani zomlemekeza.

5. Myimbireni Yehova zomlemekeza ndizeze;Ndi zeze ndi mau a salmo.

6. Pfuulani pamaso pa Mfumu Yehova,Ndi mbetete ndi liu la lipenga,

7. Nyanja Ipfuule ndi kudzala kwace;Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8. Mitsinje iombe manja;Mapiri apfuule pamodzi mokondwera;

9. Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu molunjika,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 98