4. Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;Kuwitsani ndi kupfuulira mokondwera; inde, yimbirani zomlemekeza.
5. Myimbireni Yehova zomlemekeza ndizeze;Ndi zeze ndi mau a salmo.
6. Pfuulani pamaso pa Mfumu Yehova,Ndi mbetete ndi liu la lipenga,
7. Nyanja Ipfuule ndi kudzala kwace;Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;
8. Mitsinje iombe manja;Mapiri apfuule pamodzi mokondwera;
9. Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu molunjika,