7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,
8. Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.
9. Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.
10. Nenani mwa amitundu, Yehova acita ufumu;Dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;Adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.
11. Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;Nyanja ibume mwa kudzala kwace:
12. Munda ukondwerere ndi zonse ziri m'mwemo;Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera;
13. Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi:Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu ndi coonadi.