Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 96:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace;Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.

3. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu;Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

4. Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.

5. Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano:Koma Yehova analenga zakumwamba.

6. Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu:M'malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.

7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 96