Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 96:2-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace;Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.

3. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu;Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

4. Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.

5. Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano:Koma Yehova analenga zakumwamba.

6. Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu:M'malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.

7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

8. Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.

9. Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.

10. Nenani mwa amitundu, Yehova acita ufumu;Dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;Adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11. Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;Nyanja ibume mwa kudzala kwace:

12. Munda ukondwerere ndi zonse ziri m'mwemo;Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera;

13. Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi:Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu ndi coonadi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 96