Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 96:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Nenani mwa amitundu, Yehova acita ufumu;Dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;Adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11. Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;Nyanja ibume mwa kudzala kwace:

12. Munda ukondwerere ndi zonse ziri m'mwemo;Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera;

13. Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi:Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu ndi coonadi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 96