Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 96:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano;Myimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2. Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace;Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.

3. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu;Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

4. Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.

5. Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano:Koma Yehova analenga zakumwamba.

6. Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu:M'malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.

7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

8. Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.

9. Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 96