1. Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano;Myimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.
2. Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace;Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.
3. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu;Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.
4. Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.
5. Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano:Koma Yehova analenga zakumwamba.
6. Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu:M'malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.
7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,