Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 94:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu wakubwezera cilango,Yehova, Mulungu wakubwezera cilango, muoneke wowala.

2. Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi:Bwezerani odzikuza coyenera iwo.

3. Oipa adzatumpha ndi cimwemwe kufikira liti, Yehova?Oipa adzatero kufikira liti?

4. Anena mau, alankhula zawawa;Adzitamandira onse ocita zopanda pace.

5. Aphwanya anthu anu, Yehova,Nazunza colandira canu.

6. Amapha wamasiye ndi mlendo,Nawapha ana amasiye.

7. Ndipo amati, Yehova sacipenya,Ndi Mulungu wa Yakobo sacisamalira.

8. Zindikirani, opulukira inu mwa anthu;Ndipo opusa inu, mudzacita mwanzeru liti?

9. Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva?Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

10. Kodi Iye wakulangiza mitundu ya anthu, ndiye wosadzudzula?Si ndiye amene aphunzitsa munthu nzeru?

Werengani mutu wathunthu Masalmo 94