8. Koma Inu, Yehova, muli m'mwamba ku nthawi yonse.
9. Pakuti, taonani, adani anu, Yehova,Pakuti, taonani, adani anu adzatayika;Ocita zopanda pace onse adzamwazika.
10. Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati;Anandidzoza mafuta atsopano.
11. Diso langa lapenya cokhumba ine pa iwo ondilalira,M'makutu mwanga ndamva cokhumba ine pa iwo akucita zoipa akundiukira.
12. Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa;Adzakula ngati mkungudza wa ku Lebano.
13. Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova,Adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.
14. Atakalamba adzapatsanso zipatso;Adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri:
15. Kulalikira kuti Yehova ngwolunjika;Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe cosalungama.