Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 91:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.

8. Koma udzapenya ndi maso ako,Nudzaona kubwezera cilango oipa.

9. Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo pangaUdaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;

10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11. Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe,Akusunge m'njira zako zonse.

12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.

13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

Werengani mutu wathunthu Masalmo 91