Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 91:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11. Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe,Akusunge m'njira zako zonse.

12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.

13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

14. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.

15. Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha;Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.

16. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 91