Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 91:1-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Iye amene akhala pansi m'ngaka yace ya Wam'mwambamwambaAdzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

2. Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa;Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira,

3. Pakuti adzakuonjola ku msampha wa msodzi,Ku mliri wosakaza.

4. Adzakufungatira ndi nthenga zace,Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace;Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.

5. Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;

6. Kapena mliri woyenda mumdima,Kapena cionongeko cakuthera usana.

7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.

8. Koma udzapenya ndi maso ako,Nudzaona kubwezera cilango oipa.

9. Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo pangaUdaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;

10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11. Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe,Akusunge m'njira zako zonse.

12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.

13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

14. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.

15. Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha;Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.

16. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,

Werengani mutu wathunthu Masalmo 91