Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 90:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ambuye, Inu munatikhalira mokhalamoM'mibadwo mibadwo.

2. Asanabadwe mapiri,Kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu,Inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha,Inu ndinu Mulungu.

3. Mubweza munthu akhale pfumbi;Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.

4. Pakuti pamaso panu zaka zikwiZikhala ngati dzulo, litapita,Ndi monga ulonda wa usiku.

5. Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo;Mamawa akhala ngati msipu waphuka.

6. Mamawa uphuka bwino;Madzulo ausenga, nuuma.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 90