Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 9:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti mwandiweruzira mlandu wanga;Mwakhala pa mpando wacifumu, Woweruza wolungama.

5. Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo,Mwafafaniza dzina lao ku nthawi Yomka muyaya.

6. Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse;Ndipo midziyo mwaipasula,Cikumbukilo cao pamodzi catha.

7. Koma Yehova akhala cikhalire:Anakonzeratu mpando wacifumu wace kuti aweruze.

8. Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m'cilungamo,Nadzaweruza anthu molunjika.

9. Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi.Msanje m'nyengo za nsautso;

10. Ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu;Pakuti, Inu Yehova, simunawasiya iwo akufuna Inu.

11. Yimbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni;Lalikirani mwa anthu nchito zace.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 9