Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 9:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba:Lakodwa phazi lao muukonde anaucha.

16. Anadziwika Yehova, anacita kuweruza:Woipayo anakodwa ndi nchito ya manja ace.

17. Oipawo adzabwerera kumanda,Inde amitundu onse akuiwala Mulungu.

18. Pakuti sadzaiwalika nthawi zonse waumphawi,Kapena ciyembekezo ca ozunzika sicidzaonongeka kosatha.

19. Ukani, Yehova, asalimbike munthu;Amitundu aweruzidwe pankhope panu.

20. Muwacititse mantha, Yehova; Adziwe amitundu kuti ali anthu.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 9