Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 9:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse;Ndidzawerengera zodabwiza zanu zonse.

2. Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu;Ndidzayimbira dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

3. Pobwerera m'mbuyo adani anga,Akhumudwa naonongeka pankhope panu,

4. Pakuti mwandiweruzira mlandu wanga;Mwakhala pa mpando wacifumu, Woweruza wolungama.

5. Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo,Mwafafaniza dzina lao ku nthawi Yomka muyaya.

6. Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse;Ndipo midziyo mwaipasula,Cikumbukilo cao pamodzi catha.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 9