Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Masalmo 85:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Kodi simudzatipatsanso moyo,Kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7. Tionetseni cifundo canu, Yehova,Tipatseni cipulumutso canu.

8. Ndidzamva colankhula Mulungu Yehova;Pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ace, ndi okondedwa ace;Koma asabwererenso kucita zapusa.

9. Indedi cipulumutso cace ciri pafupi ndi iwo akumuopa Iye;Kuti m'dziko mwathu mukhale ulemu.

10. Cifundo ndi coonadi zakomanizana;Cilungamo ndi mtendere zapsompsonana,

11. Coonadi ciphukira m'dziko;Ndi cilungamo casuzumira ciri m'mwamba.

12. Inde Yehova adzapereka zokoma;Ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zace.

13. Cilungamo cidzamtsogolera; Nicidzamkonzera mapazi ace njira.

Werengani mutu wathunthu Masalmo 85