8. Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,
9. Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:
10. Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.
11. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:
12. Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.
13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.
14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;
15. Momwemo muwatsate ndi namondwe,Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.
16. Acititseni manyazi pankhope pao;Kuti afune dzina lanu, Yehova.
17. Acite manyazi, naopsedwe kosatha;Ndipo asokonezeke, naonongeke: